MASALIMO 83
83
Amitundu apangana kuononga Aisraele. Apempha Mulungu awalanditse
Nyimbo. Salimo la Asafu.
1 #
Mas. 109.1
Mulungu musakhale chete;
musakhale duu, osanena kanthu, Mulungu.
2 #
Mac. 4.25
Pakuti taonani, adani anu aphokosera,
ndipo okwiyira Inu aweramutsa mutu.
3Apangana mochenjerera pa anthu anu,
nakhalira upo pa obisika anu.
4 #
Est. 3.6, 9 Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu;
ndipo dzina la Israele lisakumbukikenso.
5Pakuti anakhalira upo ndi mtima umodzi;
anachita chipangano cha pa Inu.
6Mahema a Edomu ndi a Aismaele;
Mowabu ndi Ahagiri;
7Gebala ndi Amoni ndi Amaleke;
Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala m'Tiro.
8Asiriya anaphatikana nao;
anakhala dzanja la ana a Loti.
9 #
Num. 31.7; Ower. 4.15, 24 Muwachitire monga munachitira Midiyani;
ndi Sisera, ndi Yabini kumtsinje wa Kisoni,
10amene anaonongeka ku Endori;
anakhala ngati ndowe ya kumunda.
11 #
Ower. 7.25; 8.5-21 Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;
mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna,
12amene anati, Tilande malo okhalamo Mulungu, akhale athu.
13Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;
ngati ziputu zomka ndi mphepo.
14Monga moto upsereza nkhalango,
ndi monga lawi liyatsa mapiri.
15Momwemo muwatsate ndi namondwe,
nimuwaopse ndi kamvulumvulu wanu.
16 #
Mas. 35.4, 26 Achititseni manyazi pankhope pao;
kuti afune dzina lanu, Yehova.
17Achite manyazi, naopsedwe kosatha;
ndipo asokonezeke, naonongeke.
18Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova,
ndinu Wam'mwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Currently Selected:
MASALIMO 83: BLPB2014
Highlight
Share
Copy
Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi