MASALIMO 82
82
Oweruza aweruza bwino
Salimo la Asafu.
1Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu,
aweruza pakati pa milungu.
2 #
Deut. 1.17; Miy. 18.5 Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti,
ndi kusamalira nkhope ya oipa?
3 #
Yer. 22.3
Weruzani osauka ndi amasiye;
weruzani molungama ozunzika ndi osowa.
4Pulumutsani osauka ndi aumphawi;
alanditseni m'dzanja la oipa.
5 #
Mik. 3.1-2
Sadziwa, ndipo sazindikira;
amayendayenda mumdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 #
Yoh. 10.34
Ndinati Ine, Inu ndinu milungu,
ndi ana a Wam'mwambamwamba nonsenu.
7Komatu mudzafa monga anthu,
ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.
8 #
Mas. 2.8
Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi;
pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.
Currently Selected:
MASALIMO 82: BLPB2014
Highlight
Share
Copy
Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi