MASALIMO 76
76
Ulemerero ndi mphamvu ya Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Neginoto. Salimo la Asafu. Nyimbo.
1Mulungu adziwika mwa Yuda,
dzina lake limveka mwa Israele.
2 #
Gen. 14.18
Msasa wake unali m'Salemu,
ndipo pokhala Iye m'Ziyoni.
3 #
Ezk. 39.9
Pomwepo anathyola mivi ya pauta;
chikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.
4Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka
wakuposa mapiri muli achifwamba.
5Olimba mtima chifunkhidwa chuma chao, agona tulo tao;
amuna onse amphamvu asowa manja ao.
6 #
Eks. 15.1, 21 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,
galeta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.
7 #
Nah. 1.6
Inu ndinu woopsa;
ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala chilili ndani pamaso panu?
8 #
Ezk. 38.19-20
Mudamveketsa chiweruzo chochokera Kumwamba;
dziko lapansi linachita mantha, nilinakhala chete,
9pakuuka Mulungu kuti aweruze,
kuti apulumutse ofatsa onse a pa dziko lapansi.
10 #
Eks. 9.16
Indedi, kuzaza kwake kwa munthu kudzakulemekezani;
chotsalira cha kuzazaku mudzachiletsa.
11 #
Mas. 50.14
Windani ndipo chitirani Yehova Mulungu wanu zowindazo;
onse akumzinga abwere nacho chopereka
cha kwa Iye amene ayenera kumuopa.
12Iye adzadula mzimu wa akulu;
akhala woopsa kwa mafumu a pa dziko lapansi.
Currently Selected:
MASALIMO 76: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi