MASALIMO 75
75
Mulungu woweruza asiyanitsa pakati pa odzikuza ndi olungama
Kwa Mkulu wa Nyimbo; Altasyeti; Salimo la Asafu. Nyimbo.
1Tikuyamikani Inu, Mulungu;
tiyamika, pakuti dzina lanu lili pafupi;
afotokozera zodabwitsa zanu.
2Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.
3Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo;
ndinachirika mizati yake.
4Ndinati kwa odzitamandira,
musamachita zodzitamandira;
ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;
5musamakwezetsa nyanga yanu;
musamalankhula ndi khosi louma.
6Pakuti kukuzaku sikuchokera kum'mawa,
kapena kumadzulo, kapena kuchipululu.
7 #
Mas. 50.6; 1Sam. 2.7 Pakuti Mulungu ndiye woweruza;
achepsa wina, nakuza wina.
8 #
Mas. 60.3
Pakuti m'dzanja la Yehova muli chikho;
ndi vinyo wake achita thovu;
chidzala ndi zosanganizira, ndipo atsanulako.
Indedi, oipa onse a pa dziko lapansi adzamwa
nadzagugudiza nsenga zake.
9Koma ine ndidzalalikira kosalekeza,
ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.
10 #
Mas. 89.17; Yer. 48.25 Ndipo ndidzatseteka nyanga zonse za oipa;
koma nyanga za wolungama zidzakwezeka.
Currently Selected:
MASALIMO 75: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi