HOSEYA 6
6
Israele abwerera kunka kwa Yehova
1 #
1Sam. 2.6; Yer. 30.17 Tiyeni, tibwerere kunka kwa Yehova; pakuti wang'amba, nadzatipoletsera; wakantha, nadzatimanga. 2Atapita masiku awiri adzatitsitsimutsa, tsiku lachitatu adzatiutsa; ndipo tidzakhala ndi moyo pamaso pake. 3#Yob. 29.23; Yes. 54.13; Yoh. 7.17Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kutuluka kwake kwakonzekeratu ngati matanda kucha; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.
Efuremu ndi Yuda adzudzulidwa
4 #
Hos. 13.3
Efuremu iwe, ndidzakuchitira chiyani? Yuda iwe, ndikuchitire chiyani? Pakuti kukoma mtima kwako kukunga mtambo wam'mawa ndi ngati mame akuphawa mamawa. 5Chifukwa chake ndawalikha mwa aneneri; ndawapha ndi mau a pakamwa panga; ndi maweruzo anga atuluka ngati kuunika. 6#1Sam. 15.22; Mas. 50.8-9; Mat. 9.13; 12.7; Yoh. 17.3Pakuti ndikondwera nacho chifundo, si nsembe ai; ndi kumdziwa Mulungu kuposa nsembe zopsereza. 7Koma iwo analakwira chipangano ngati Adamu, m'mene anandichitira monyenga. 8Giliyadi ndiwo mudzi wa ochita zoipa, wa mapazi a mwazi. 9#Hos. 5.1-2Ndipo monga magulu a mbala alalira munthu, momwemo msonkhano wa ansembe amapha pa njira ya ku Sekemu; indedi achita choipitsitsa. 10#Yer. 5.30-31M'nyumba ya Israele ndinaona chinthu choopsetsa; pamenepo pali uhule wa Efuremu; Israele wadetsedwa. 11#Yer. 51.33Akuikidwiratunso nyengo yakukolola, Yuda iwe, pamene ndikabwezanso undende wa anthu anga.
Currently Selected:
HOSEYA 6: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi