NYIMBO YA SOLOMONI 5
5
1 #
Mas. 36.8
Ndalowa m'munda mwanga, mlongo wanga, mkwatibwi:
Ndatchera mure wanga ndi zonunkhiritsa zanga;
ndadya uchi wanga ndi chisa chake;
ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.
Idyani, atsamwalinu,
imwani, mwetsani chikondi.
Alekana nthawi
2 #
Chiv. 3.20; Yoh. 3.29 Ndinagona tulo, koma mtima wanga unali maso:
Ndi mau a bwenzi langa mnyamatayo agogoda, nati,
nditsegulire, mlongo wanga, wokondedwa wanga,
nkhunda yanga, wangwiro wanga:
Pakuti pamtu panga padzala mame,
patsitsi panga pali madontho a usiku.
3Ndinayankha kuti, Ndavula malaya anga, ndiwavalenso bwanji?
Ndasuka mapazi anga; ndiwadetserenji?
4Bwenzi langa analonga dzanja lake pazenera,
mtima wanga ndi kuguguda chifukwa cha iye.
5Ndinauka ndikatsegulire bwenzi langa;
pamanja panga panakha mure.
Ndi pa zala zanga madzi a mure,
pa zogwirira za mpikizo.
6Ndinamtsegulira bwenzi langalo;
koma ndinampeza, bwenzi langa atachoka.
Moyo wanga unalefuka polankhula iye:
Ndinamfunafuna, osampeza;
ndinamuitana, koma sanandivomere.
7Alonda akuyenda m'mudzi anandipeza,
nandikantha, nanditema;
osunga makoma nandichotsera chophimba changa.
8Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,
mukapeza bwenzi langa, mudzamuuza chiyani?
Kuti ndadwala ndi chikondi.
9Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,
mkaziwe woposa kukongola?
Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji,
kuti utilumbirira motero?
10 #
Mas. 45.2; Yoh. 1.14 Wokondedwa wanga ali woyera ndi wofiira,
womveka mwa zikwi khumi.
11Mutu wake ukunga golide, woyengetsa,
tsitsi lake lopotana, ndi lakuda ngati khungubwi.
12Ana a maso ake akunga nkhunda
pambali pa mitsinje ya madzi;
otsukidwa ndi mkaka, okhala pa mitsinje yodzala.
13Masaya ake akunga chitipula chobzalamo ndiwo,
ngati mitumbira yoyangapo masamba onunkhira:
Milomo yake ikunga akakombo, pakukhapo madzi a mure.
14Manja ake akunga zing'anda zagolide
zoikamo zonyezimira zoti biriwiri.
Thupi lake likunga chopanga cha minyanga
cholemberapo masafiro.
15Miyendo yake ikunga zoimiritsa za mwala wonyezimira,
zogwirika m'kamwa mwa golide:
Maonekedwe ake akunga Lebanoni,
okometsetsa ngati mikungudza.
16M'kamwa mwake muli mokoma; inde,
ndiye wokondweretsa ndithu.
Ameneyu ndi wokondedwa wanga,
ameneyu ndi bwenzi langa,
ana akazi inu a ku Yerusalemu.
Currently Selected:
NYIMBO YA SOLOMONI 5: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi