YOSWA 19
19
Malire a Simeoni
1 #
Yos. 19.9; Gen. 49.5, 7 Ndipo maere achiwiri anamtulukira Simeoni, fuko la ana a Simeoni monga mwa mabanja ao; ndi cholowa chao chinali pakati pa cholowa cha ana a Yuda. 2Ndipo anali nacho cholowa chao Beereseba, kapena Sheba, ndi Molada; 3ndi Hazara-Suwala, ndi Bala, ndi Ezemu; 4ndi Elitoladi, ndi Betuli, ndi Horoma; 5ndi Zikilagi, ndi Betemara-Kaboti, ndi Hazara-Susa: 6ndi Betelebaoti, ndi Saruheni; midzi khumi ndi itatu ndi milaga yao; 7Aini, Rimoni ndi Eteri ndi Asani; midzi inai ndi milaga yao; 8ndi milaga yonse yozungulira midzi iyi mpaka Baalati-Bere ndiwo Rama kumwera. Ndicho cholowa cha fuko la ana a Simeoni, monga mwa mabanja ao. 9#Yos. 19.1M'gawo la ana a Yuda muli cholowa cha ana a Simeoni; popeza gawo la ana a Yuda linawachulukira; chifukwa chake ana a Simeoni anali nacho cholowa pakati pa cholowa chao.
Malire a Zebuloni
10Ndipo maere achitatu anakwerera ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao; ndi malire a cholowa chao anafikira ku Saridi; 11nakwera malire ao kunka kumadzulo ndi ku Mareyala nafikira ku Dabeseti, nafikira ku mtsinje wa patsogolo pa Yokoneamu; 12ndi kuchokera ku Saridi anazungulira kunka kum'mawa kumatulukira dzuwa, mpaka malire a Kisiloti-Tabori; natuluka kunka ku Daberati, nakwera ku Yafiya; 13ndi pochoka pamenepo anapitirira kunka kum'mawa ku Gatihefere, ku Etikazini; natuluka ku Rimoni umene ulembedwa mpaka ku Neya, 14nauzungulira malire kumpoto, kunka ku Hanatoni; ndi matulukiro ake anali ku chigwa cha Ifutahele; 15ndi Katati, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi milaga yao. 16Ichi ndi cholowa cha ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi milaga yao.
Malire a Isakara
17Maere achinai anamtulukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao. 18Ndi malire ao anali ku Yezireele, ndi Kesuloti, ndi Sunemu; 19ndi Hafaraimu, ndi Siyoni, ndi Anaharati; 20ndi Rabiti ndi Kisiyoni, ndi Ebezi; 21ndi Remeti ndi Enganimu ndi Enihada, ndi Betepazezi; 22ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi matulukiro a malire ao anali ku Yordani; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi milaga yao. 23Ichi ndi cholowa cha fuko la ana a Isakara, monga mwa mabanja ao, midzi ndi milaga yao.
Malire a Asere
24Ndipo maere achisanu analitulukira fuko la ana a Asere monga mwa mabanja ao. 25Ndi malire ao ndiwo Helekati, ndi Hali, ndi Beteni ndi Akisafu; 26#1Maf. 18.19-20ndi Alamumeleki, ndi Amada, ndi Misala; nafikira ku Karimele kumadzulo ndi ku Sihori-Libinati; 27nazungulira kotulukira dzuwa ku Betedagoni, nafikira ku Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifutahele, kumpoto ku Betemeke, ndi Neiyeli; natulukira ku Kabulu kulamanzere, 28ndi Ebroni, ndi Rehobu, ndi Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni wamkulu; 29#2Sam. 5.11nazungulira malire kunka ku Rama, ndi kumudzi wa linga la Tiro; nazungulira malire kunka ku Hosa; ndi matulukiro ake anali kunyanja, kuchokera ku Mahalabu mpaka ku Akizibu; 30Uma womwe ndi Afeki, ndi Rehobu; midzi makumi awiri mphambu iwiri ndi milaga yao. 31Ichi ndi cholowa cha fuko la ana a Asere monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi milaga yao.
Malire a Nafutali
32Maere achisanu ndi chimodzi anatulukira ana a Nafutali, ana a Nafutali monga mwa mabanja ao. 33Ndipo malire ao anayambira ku Helefe ku thundu wa ku Zaananimu, ndi Adami-Nekebu, ndi Yabinele, mpaka ku Lakumu; ndi matulukiro ake anali ku Yordani; 34nazungulira malire kunka kumadzulo ku Azinoti-Tabori, natulukira komweko kunka ku Hukoku; nafikira ku Zebuloni kumwera, nafikira ku Asere kumadzulo, ndi ku Yuda pa Yordani kum'mawa. 35Ndipo midzi yamalinga ndiyo Zidimu, Zeri, ndi Hamati, Rakati, ndi Kinereti; 36ndi Adama, ndi Rama, ndi Hazori; 37ndi Kedesi, ndi Ederei, ndi Enihazori; 38ndi Yironi, ndi Migidalele, Horemu, ndi Betanati, ndi Betesemesi; midzi khumi ndi isanu ndi inai, ndi milaga yao. 39Ichi ndi cholowa cha fuko la ana a Nafutali, monga mwa mabanja ao, midzi ndi milaga yao.
Malire a Dani
40Maere achisanu ndi chiwiri anatulukira fuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao. 41Ndipo malire a cholowa chao anali Zora, ndi Esitaoli, ndi Irisemesi; 42Saalabini, ndi Ayaloni ndi Itila; 43ndi Eloni ndi Timna ndi Ekeroni; 44ndi Eliteke, ndi Gibetoni, ndi Baalati; 45ndi Yehudi, ndi Beneberaki, ndi Gatirimoni; 46#Mac. 9.36ndi Meyarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pa Yopa. 47#Ower. 18.29Koma malire a ana a Dani anatuluka kupitirira iwowa; pakuti ana a Dani anakwera nathira nkhondo ku Lesemu, naulanda naukantha ndi lupanga lakuthwa, naulandira, nakhala m'mwemo, nautcha Lesemu, Dani; ndilo dzina la Dani atate wao. 48Ichi ndi cholowa cha fuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi milaga yao.
Cholowa cha Yoswa
49Ndipo atatha kuligawa dziko likhale cholowa chao monga mwa malire ake, ana a Israele anapatsa Yoswa mwana wa Nuni cholowa pakati pao; 50#Yos. 24.30monga mwa lamulo la Yehova anampatsa mudzi umene anawapempha, ndiwo Timnati-Sera, ku mapiri a Efuremu; ndipo anamanga mudziwo nakhala m'mwemo.
51 #
Yos. 18.1
Izi ndizo zolowa anazigawa Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akulu a nyumba za atate a mafuko a ana a Israele, zikhale zaozao, ndi kulota maere ku Silo pamaso pa Yehova ku khomo la chihema chokomanako. Momwemo anatha kuligawa dziko.
Currently Selected:
YOSWA 19: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi