YOSWA 15
15
Malire a Yuda
1Ndipo gawo la fuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao linafikira malire a Edomu, ku chipululu cha Zini kumwera, ku malekezero a kumwera. 2Ndi malire ao a kumwera, anayambira ku malekezero a Nyanja ya Mchere, ku nyondo yoloza kumwera; 3natuluka kumwera kwa chikweza cha Akarabimu, napitirira ku Zini, nakwera kumwera kwa Kadesi-Baranea, napitirira ku Hezironi, nakwera ku Adara, nazungulira ku Karika; 4napitirira ku Azimoni, natuluka ku mtsinje wa Ejipito; ndi malekezero a malirewa anali ku Nyanja Yaikulu; awa ndi malire anu a kumwera. 5Ndi malire a kum'mawa ndiwo Nyanja ya Mchere, mpaka mathiriro ake a Yordani. Ndi malire a kumpoto anayambira nyondo ya nyanja ku mathiriro a Yordani; 6nakwera malire kunka ku Betehogila, napitirira kumpoto kwa Betaraba; nakwera malire kunka ku mwala wa Bohani mwana wa Rubeni; 7nakwera malire kunka ku Debiri, kuchokera ku chigwa cha Akori, ndi kumpoto kupenyera Giligala ndiko kundunji kwa chikweza cha Adumimu, ndiko kumwera kwa mtsinje; napitirira malire kunka ku madzi a Enisemesi, ndi matulukiro ake anali ku Enirogele; 8nakwera malire kunka ku chigwa cha mwana wa Hinomu, kumbali kwa Ayebusi, kumwera, ndiko Yerusalemu; nakwera malire kunka kumwamba kwa phiri lokhala patsogolo pa chigwa cha Hinomu kumadzulo, ndilo ku mathero ake a chigwa cha Refaimu kumpoto. 9Ndipo analemba malire kuyambira pamwamba pa phiri mpaka chitsime cha madzi cha Nefitowa, natulukira malire kumidzi ya phiri la Efuroni; ndipo analemba malire kunka ku Baala, ndiwo Kiriyati-Yearimu. 10Ndipo malire anazungulira kuyambira ku Baala kunka kumadzulo, kuphiri la Seiri, napitirira kumbali kwa phiri la Yearimu kumpoto, ndilo Kesaloni, natsikira ku Betesemesi, napitirira ku Timna; 11natuluka malire kunka ku mbali ya Ekeroni kumpoto; ndipo analemba malire kunka ku Sikeroni, napitirira kuphiri la Baala, natuluka ku Yabinele; ndipo matulukiro a malire anali kunyanja. 12Ndi malire a kumadzulo anali ku Nyanja Yaikulu ndiwo malire ake. Awa ndi malire a ana a Yuda pozungulira monga mwa mabanja ao.
13Koma Yoswa anampatsa Kalebe mwana wa Yefune gawo mwa ana a Yuda, monga Yehova adamlamulira, ndiwo mudzi wa Araba, ndiye atate wa Anaki, ndiwo Hebroni. 14Ndipo Kalebe anaingitsako ana amuna atatu a Anaki, ndiwo Sesai, ndi Ahimani, ndi Talimai, ana a Anaki. 15Nakwera komweko kunka kwa nzika za Debiri; koma kale dzina la Debiri ndilo Kiriyati-Sefere. 16Ndipo Kalebe anati, Iye amene akantha Kiriyati-Sefere, naulanda, yemweyo ndidzampatsa Akisa mwana wanga akhale mkazi wake. 17#Ower. 1.13Ndipo Otiniyele mwana wa Kenazi, mbale wake wa Kalebe, anaulanda; ndipo anampatsa Akisa mwana wake akhale mkazi wake. 18Ndipo kunali, m'mene anamdzera, anamkangamiza mwamuna wake kuti apemphe atate wake ampatse munda; ndipo anatsika pa bulu; pamenepo Kalebe ananena naye, Ufunanji? 19Nati iye, Mundipatse dalitso; popeza mwandipatsa dziko la kumwera, ndipatseninso zitsime za madzi. Pamenepo anampatsa zitsime za kumtunda, ndi zitsime za kunsi.
20Ichi ndi cholowa cha fuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao.
21Ndipo midzi ya ku malekezero a fuko la ana a Yuda ku malire a Edomu, kumwera ndiwo, Kabizeeli ndi Edere, ndi Yaguru; 22ndi Kina ndi Dimona, ndi Adada; 23ndi Kedesi, ndi Hazori, ndi Itinani; 24Zifi ndi Telemu ndi Bealoti; 25ndi Hazori-Hadata, ndi Keriyoti-Hezironi, ndiwo Hazori; 26Amama ndi Sema ndi Molada; 27ndi Hazara-Gada, ndi Hesimoni, ndi Betepeleti; 28ndi Hazara-Suwala, ndi Beereseba, ndi Biziyotiya; 29Baala, ndi Iyimu, ndi Ezemu; 30ndi Elitoladi, ndi Kesili ndi Horoma; 31#1Sam. 27.6ndi Zikilagi, ndi Madimana ndi Sanisana; 32ndi Lebaoti, ndi Silihimu, ndi Aini ndi Rimoni; midzi yonse ndiyo makumi awiri kudza isanu ndi inai; pamodzi ndi milaga yao.
33 #
Gen. 48.19
Ku chigwa, Esitaoli, ndi Zora ndi Asina; 34ndi Zanowa, ndi Enganimu, Tapuwa, ndi Enamu; 35Yaramuti, ndi Adulamu, Soko, ndi Azeka; 36ndi Saaraimu, ndi Aditaimu, ndi Gedera, ndi Gederotaimu; midzi khumi ndi inai pamodzi ndi milaga yao.
37Zenani, ndi Hadasa, ndi Megidali-Gadi; 38#2Maf. 14.7ndi Dileani, ndi Mizipa, ndi Yokotele; 39Lakisi ndi Bozikati ndi Egiloni; 40ndi Kaboni, ndi Lahamasi, ndi Kitilisi; 41ndi Gederoti, Betedagoni, ndi Naama, ndi Makeda; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi pamodzi ndi milaga yao.
42Libina ndi Eteri ndi Asani; 43ndi Ifuta ndi Asina ndi Nezibu; 44ndi Keila ndi Akizibu, ndi Maresa; midzi isanu ndi inai pamodzi ndi milaga yao.
45Ekeroni pamodzi ndi midzi yake ndi milaga yao; 46kuyambira ku Ekeroni mpaka kunyanja, yonse ya ku mbali ya Asidodi, pamodzi ndi milaga yao.
47Asidodi, midzi yake ndi milaga yake; Gaza, midzi yake ndi milaga yake; mpaka mtsinje wa Ejipito, ndi Nyanja Yaikulu ndi malire ake.
48Ndi kumapiri Samiri, ndi Yatiri, ndi Soko; 49ndi Dana, ndi Kiriyati-Sana, ndiwo Debiri; 50ndi Anabu, ndi Esitemowa, ndi Animu; 51ndi Goseni, ndi Holoni, ndi Gilo; midzi khumi ndi umodzi pamodzi ndi milaga yao.
52Arabu, ndi Duma, ndi Esani; 53ndi Yanimu, ndi Betetapuwa, ndi Afeka; 54ndi Humata, ndi Kiriyati-Ariba, ndiwo Hebroni, ndi Ziyori; midzi isanu ndi inai pamodzi ndi milaga yao.
55Maoni, Karimele, ndi Zifi, ndi Yuta; 56ndi Yezireele, ndi Yokodeamu, ndi Zanowa; 57Kaini, Gibea ndi Timna; midzi khumi pamodzi ndi milaga yao.
58Halahulu, Betezuri, ndi Gedori, 59ndi Maarati, ndi Betanoti, ndi Elitekoni; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi milaga yao.
60Kiriyati-Baala, ndiwo Kiriyati-Yearimu ndi Raba; midzi iwiri pamodzi ndi milaga yao.
61M'chipululu, Betaraba, Midini, ndi Sekaka; 62ndi Nibisani, ndi Mudzi wa Mchere, ndi Engedi; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi milaga yao.
63 #
Ower. 1.21; 2Sam. 5.6 Koma ana a Yuda sanakhoze kuingitsa Ayebusi, nzika za Yerusalemu: m'mwemo Ayebusi anakhala pamodzi ndi ana a Yuda, ku Yerusalemu, mpaka lero lino.
Currently Selected:
YOSWA 15: BLPB2014
Highlight
Share
Copy
![None](/_next/image?url=https%3A%2F%2Fimageproxy.youversionapi.com%2F58%2Fhttps%3A%2F%2Fweb-assets.youversion.com%2Fapp-icons%2Fen.png&w=128&q=75)
Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi