YouVersion Logo
Search Icon

AMOSI 6

6
Aisraele otsata zilakolako zao adzapsinjika ndi mtundu wina wa anthu
1 # Eks. 19.5 Tsoka osalabadirawo m'Ziyoni, ndi iwo okhazikika m'phiri la Samariya, ndiwo anthu omveka a mtundu woposa wa anthu, amene nyumba ya Israele iwafikira! 2Pitani ku Kaline, nimuone; kuchokera komweko mupite ku Hamati wamkulu mutsikire ku Gati wa Afilisti; kodi awo ndi okoma koposa maufumu ano? Kapena malire ao aposa malire anu? 3#Ezk. 12.27Inu akutalikitsa tsiku loipa, ndi kusendeza pafupi mpando wachiwawa; 4ogona pamakama aminyanga, nadzithinula pa maguwa ao ogonapo, nadya anaankhosa a kuzoweta, ndi anaang'ombe ochoka pakati pa khola; 5akungoimba kutsata maliridwe a zeze, nadzilingiririra zoimbira nazo ngati Davide; 6#Gen. 37.25akumwera vinyo m'zipanda, nadzidzoza ndi mafuta abwino oposa, osagwidwa chisoni ndi kuthyoka kwa Yosefe. 7Chifukwa chake tsono, adzatengedwa ndende ndi oyamba kutengedwa ndende; ndi phokoso la iwo odzithinula lidzapita. 8#Ezk. 24.21Ambuye Yehova walumbira pali Iye mwini, ati Yehova Mulungu wa makamu, Ndinyansidwa nako kudzikuza kwa Yakobo, ndidana nazo nyumba zake zachifumu; m'mwemo ndidzapereka mudzi, ndi zonse zili m'menemo. 9Ndipo kudzachitika, mukatsala amuna khumi m'nyumba imodzi, adzafa. 10#Amo. 5.13; 8.3Ndipo mbale wake wa munthu akamnyamula, ndiye womtentha, kutulutsa mafupa m'nyumba, nakati kwa iye ali m'kati mwa nyumbamo, Atsala wina nawe kodi? Nakati Iai; pamenepo adzati, Khala chete; pakuti sitingatchule dzina la Yehova. 11Pakuti taonani, Yehova walamulira, nadzakantha nyumba yaikulu ichite mpata, ndi nyumba yaing'ono ichite mindala. 12#Amo. 5.7Kodi akavalo adzathamanga pathanthwe? Kodi adzalimako ndi ng'ombe pakuti mwasanduliza chiweruzo chikhale ndulu, ndi chipatso cha chilungamo chikhale chivumulo; 13inu okondwera nacho chopanda pake, ndi kuti, Kodi sitinadzilimbitsa tokha ndi kulanda Karinaimu mwa mphamvu yathuyathu? 14#Yer. 5.15Pakuti taonani, ndidzakuutsirani mtundu wa anthu, nyumba ya Israele, ati Yehova Mulungu wa makamu; ndipo adzakupsinjani kuyambira polowera ku Hamati kufikira mtsinje wa kuchidikha.

Currently Selected:

AMOSI 6: BLPB2014

Highlight

Share

Copy

None

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in