NYIMBO YA SOLOMONI 8
8
1Mwenzi utakhala ngati mlongo wanga,
woyamwa pa bere la amai!
Ndikadakupeza panja, ndikadakupsompsona;
osandinyoza munthu.
2Ndikadakutsogolera, kukulowetsa m'nyumba ya amai,
kuti andilange mwambo;
ndikadakumwetsa vinyo wokoleretsa,
ndi madzi a makangaza anga.
3Dzanja lamanzere lake akadanditsamiritsa kumutu,
lamanja lake ndi kundifungatira.
4Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,
muutsiranji, mugalamutsiranji chikondi,
chisanafune mwini.
5 #
Eks. 19.4
Ndaniyu achokera kuchipululu,
alikutsamira bwenzi lake?
Pa tsinde la muula ndinakugalamutsa mnyamatawe:
Pomwepo amai ako anali mkusauka nawe,
pomwepo wakukubala anali m'pakati pa iwe.
6 #
Yes. 49.16; Hag. 2.23 Undilembe pamtima pako, mokhoma chizindikiro,
nundikhomenso chizindikiro pamkono pako;
pakuti chikondi chilimba ngati imfa;
njiru imangouma ngati manda:
Kung'anima kwake ndi kung'anima kwa moto,
ngati mphezi ya Yehova.
7 #
Miy. 6.35; Aef. 5.28 Madzi ambiri sangazimitse chikondi,
ngakhale mitsinje yodzala kuchikokolola:
Mwamuna akapereka katundu yense wa m'nyumba yake
ngati sintho la chikondi,
akanyozedwa ndithu.
8Tili ndi mlongwathu wamng'ono,
alibe mawere;
timchitirenji mlongo wathu
tsiku lokhoma unkhoswe wake?
9Ngati ndiye khoma, tidzamanga pa iye nsanja yasiliva:
Ngati ndiye chitseko tidzamtsekereza ndi matabwa amikungudza.
10Ndine khoma, mawere anga akunga nsanja zake:
Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.
11Solomoni anali ndi munda wamipesa ku Baala-Hamoni;
nabwereka alimi mundawo;
yense ambwezere ndalama chikwi chifukwa cha zipatso zake.
12Koma munda wanga wamipesa,
uli pamaso panga ndiwo wangatu;
nacho chikwicho, Solomoni iwe,
koma olima zipatso zake azilandira mazana awiri.
13Namwaliwe wokhala m'minda,
anzako amvera mau ako:
Nanenanso undimvetse.
14 #
Chiv. 22.17, 20 Dzifulumira, mnyamatawe wokondedwa wanga,
dzifanane ngati mphoyo pena mwana wa mbawala
pa mapiri a mphoka.
Currently Selected:
NYIMBO YA SOLOMONI 8: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi