MASALIMO 96
96
Onse a pansi pano ndi am'mwamba omwe alemekeze Mulungu
1 #
Mas. 33.3
Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano;
muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.
2Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake;
lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3Fotokozerani ulemerero wake mwa amitundu;
zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.
4 #
Mas. 95.3
Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;
ayenera amuope koposa milungu yonse.
5Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano,
koma Yehova analenga zakumwamba.
6 #
Mas. 29.1-2
Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu.
M'malo opatulika mwake muli mphamvu ndi zochititsa kaso.
7Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,
mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lake;
bwerani nacho chopereka, ndipo fikani kumabwalo ake.
9 #
Mas. 29.1-2
Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa,
njenjemerani pamaso pake, inu dziko lonse lapansi.
10 #
Mas. 93.1
Nenani mwa amitundu, Yehova achita ufumu;
dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;
adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.
11 #
Mas. 69.34
Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;
nyanja ibume mwa kudzala kwake.
12Munda ukondwerere ndi zonse zili m'mwemo;
pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzafuula mokondwera.
13 #
Mas. 67.4
Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;
pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi
Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo,
ndi mitundu ya anthu ndi choonadi.
Currently Selected:
MASALIMO 96: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi