1
YESAYA 9:6
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzamutcha dzina lake Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.
Compare
Explore YESAYA 9:6
2
YESAYA 9:2
Anthu amene anayenda mumdima, aona kuwala kwakukulu; iwo amene anakhala m'dziko la mthunzi wa imfa, kuwala kwatulukira kwa iwo.
Explore YESAYA 9:2
3
YESAYA 9:7
Za kuenjezera ulamuliro wake, ndi za mtendere sizidzatha pa mpando wachifumu wa Davide, ndi pa ufumu wake, kuukhazikitsa, ndi kuuchirikiza ndi chiweruziro ndi chilungamo kuyambira tsopano ndi kunkabe nthawi zonse. Changu cha Yehova wa makamu chidzachita zimenezi.
Explore YESAYA 9:7
4
YESAYA 9:5
Pakuti zida zonse za mwamuna wovala zida za nkhondo m'phokosomo, ndi zovala zovimvinika m'mwazi, zidzakhala zonyeka ngati nkhuni.
Explore YESAYA 9:5
5
YESAYA 9:1
Koma kumene kunali nsautso sikudzakhala kuziya. Poyamba paja Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni, ndi dziko la Nafutali, koma potsiriza pake Iye analichitira ulemu, pa khwalala la kunyanja, patsidya pa Yordani, Galileya wa amitundu.
Explore YESAYA 9:1
6
YESAYA 9:3
Inu mwachulukitsa mtundu, inu mwaenjezera kukondwa kwao; iwo akondwa pamaso panu monga akondwera m'masika, monga anthu akondwa pogawana zofunkha.
Explore YESAYA 9:3
7
YESAYA 9:4
Pakuti goli la katundu wake, ndi mkunkhu wa paphewa pake, ndodo ya womsautsa, inu mwazithyola monga tsiku la Midiyani.
Explore YESAYA 9:4
Home
Bible
Plans
Videos