1
YOHANE 19:30
Buku Lopatulika
Pamene Yesu tsono adalandira vinyo wosasayo anati, Kwatha; ndipo anawerama mutu, napereka mzimu.
Qhathanisa
Hlola YOHANE 19:30
2
YOHANE 19:28
Chitapita ichi Yesu, podziwa kuti zonse zidatha pomwepo kuti lembo likwaniridwe, ananena, Ndimva ludzu.
Hlola YOHANE 19:28
3
YOHANE 19:26-27
Pamenepo Yesu pakuona amake, ndi wophunzira amene anamkonda, alikuimirirako, ananena kwa amake, Mkazi, taonani, mwana wanu! Pamene ananena kwa wophunzirayo, Taona, amai wako. Ndipo kuyambira ora lomweli wophunzirayo ananka naye kwao.
Hlola YOHANE 19:26-27
4
YOHANE 19:33-34
koma pofika kwa Yesu, m'mene anamuona Iye, kuti wafa kale, sanathyole miyendo yake; koma mmodzi wa asilikali anamgwaza ndi nthungo m'nthiti yake, ndipo panatuluka pomwepo mwazi ndi madzi.
Hlola YOHANE 19:33-34
5
YOHANE 19:36-37
Pakuti izi zinachitika, kuti lembo likwaniridwe, Fupa la Iye silidzathyoledwa. Ndipo linenanso lembo lina, Adzayang'ana pa Iye amene anampyoza.
Hlola YOHANE 19:36-37
6
YOHANE 19:17
ndipo anasenza mtanda yekha, natuluka kunka kumalo otchedwa Malo a Bade, amene atchedwa mu Chihebri, Gologota
Hlola YOHANE 19:17
7
YOHANE 19:2
Ndipo asilikali, m'mene analuka korona waminga anamveka pamutu pake, namfunda Iye malaya achibakuwa
Hlola YOHANE 19:2
Ikhaya
IBhayibheli
Amapulani
Amavidiyo