1
Yoh. 1:12
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Komabe ena adaamlandira nakhulupirira dzina lake, ndipo ameneŵa Iye adaŵapatsa mphamvu zoti akhale ana a Mulungu.
Ṣe Àfiwé
Ṣàwárí Yoh. 1:12
2
Yoh. 1:1
Pachiyambi pa zonse Iye amene amatchedwa dzina loti Mau, anali alipo kale. Anali kwa Mulungu, ndipo anali Mulungu.
Ṣàwárí Yoh. 1:1
3
Yoh. 1:5
Kuŵalako kukuunikabe mu mdima, ndipo mdima sudathe kugonjetsa kuŵalako.
Ṣàwárí Yoh. 1:5
4
Yoh. 1:14
Wotchedwa Mau uja adasanduka munthu, nadzakhala pakati pathu. Anali wokoma mtima ndi wokhulupirika kwabasi. Ndipotu tidaona ulemerero wake, ndiye kuti ulemerero womwe Iye amalandira kwa Atate pokhala Mwana wao mmodzi yekha uja.
Ṣàwárí Yoh. 1:14
5
Yoh. 1:3-4
Mulungu adalenga zonse kudzera mwa Iye, ndipo palibe chilichonse chimene chidalengedwa popanda Iye. Mwa Iyeyo munali moyo, ndipo moyowo unali kuŵala kounikira anthu.
Ṣàwárí Yoh. 1:3-4
6
Yoh. 1:29
M'maŵa mwake Yohane adaona Yesu akubwera kwa iye, ndipo adati, “Suuyu Mwanawankhosa wa Mulungu uja, wochotsa machimo a anthu a pa dziko lonse lapansi.
Ṣàwárí Yoh. 1:29
7
Yoh. 1:10-11
Wotchedwa Mauyo anali m'dziko lapansi, ndipo Mulungu adalenga dziko lapansilo kudzera mwa Iye, komabe anthu apansipano sadamzindikire. Adaabwera kwao ndithu, koma anthu ake omwe sadamlandire.
Ṣàwárí Yoh. 1:10-11
8
Yoh. 1:9
Kuŵala kwenikweni, kounikira anthu onse, kunkadza pansi pano.
Ṣàwárí Yoh. 1:9
9
Yoh. 1:17
Paja Mulungu adatipatsa Malamulo ake kudzera mwa Mose, koma kudzera mwa Yesu Khristu adatizindikiritsa kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake.
Ṣàwárí Yoh. 1:17
Ilé
Bíbélì
Àwon ètò
Àwon Fídíò