1
Lk. 17:19
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Kenaka Yesu adauza munthuyo kuti, “Nyamuka, pita. Chikhulupiriro chako chakuchiritsa.”
Порівняти
Дослідити Lk. 17:19
2
Lk. 17:4
Akakuchimwira kasanunkaŵiri pa tsiku, nabwera kasanunkaŵiri kudzanena kuti, ‘Pepani,’ umkhululukire ndithu.”
Дослідити Lk. 17:4
3
Lk. 17:15-16
Tsono mmodzi mwa iwo, ataona kuti wachira, adabwerera nayamba kuyamika Mulungu mokweza mau. Adagwada nkuŵerama kwambiri pamaso pa Yesu, namthokoza. Koma munthuyo anali Msamariya.
Дослідити Lk. 17:15-16
4
Lk. 17:3
Chenjerani tsono! “Mbale wako akachimwa, umdzudzule. Akatembenuka mtima, umkhululukire.
Дослідити Lk. 17:3
5
Lk. 17:17
Apo Yesu adati, “Kodi achira aja si khumi? Nanga asanu ndi anai ena aja ali kuti?
Дослідити Lk. 17:17
6
Lk. 17:6
Koma Ambuye adati, “Mukadakhala ndi chikhulupiriro ngakhale chochepa kwambiri ngati kambeu ka mpiru, bwenzi mutauza mkuyu uwu kuti, ‘Zuka, kadzibzale m'nyanja,’ ndipo ukadakumverani ndithu.”
Дослідити Lk. 17:6
7
Lk. 17:33
Aliyense woyesa kudzisungira moyo wake, adzautaya, koma woutaya adzausunga.
Дослідити Lk. 17:33
8
Lk. 17:1-2
Yesu adauza ophunzira ake kuti, “Zochimwitsa anthu sizingalephere kuwoneka, koma tsoka kwa munthu wobwera nazoyo. Kukadakhala kwabwino kuti ammangirire chimwala cha mphero m'khosi ndi kukamponya m'nyanja, kupambana kuti achimwitse mmodzi mwa ana ang'onoang'onoŵa.
Дослідити Lk. 17:1-2
9
Lk. 17:26-27
“Monga momwe zidaachitikira pa nthaŵi ya Nowa, zidzateronso pa nthaŵi ya Mwana wa Munthu. Masiku amenewo anthu ankangodya ndi kumwa, ankakwatira ndi kumakwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa adaloŵa m'chombo. Pamenepo chigumula chidafika nkuŵaononga onse.
Дослідити Lk. 17:26-27
Головна
Біблія
Плани
Відео