1
Gen. 22:14
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Abrahamu adaŵatcha malowo kuti Chauta adapatsa. Ndipo mpaka lero lino anthu amati, “Paphiri la Chauta adzapatsa.”
ತಾಳೆಮಾಡಿ
Gen. 22:14 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
2
Gen. 22:2
Mulungu adati, “Tenga Isaki, mwana wako mmodzi yekha uja amene umamkonda kwambiri, upite ku dziko la Moriya. Kumeneko ukampereke ngati nsembe yopsereza pa phiri limene ndidzakuuza.”
Gen. 22:2 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
3
Gen. 22:12
“Usamuphe mnyamatayo, kapena kumchita kanthu kena kalikonse. Ndikudziŵa kuti ndiwe womveradi Mulungu, chifukwa sudandimane mwana wako mmodzi yekhayo.”
Gen. 22:12 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
4
Gen. 22:8
Abrahamu adamuyankha kuti, “Mwana wanga, Mulungu akatipatsa mwanawankhosayo.” Choncho onse aŵiri adapitiriza ulendo wao limodzi.
Gen. 22:8 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
5
Gen. 22:17-18
Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati nyenyezi zakumwamba, kapenanso ngati mchenga wa m'mbali mwa nyanja. Zidzukulu zakozo zidzagonjetsa adani ao onse. Ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalandira madalitso kudzera mwa zidzukulu zako, chifukwa iwe wandimvera.’ ”
Gen. 22:17-18 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
6
Gen. 22:1
Pambuyo pake Mulungu adamuyesa Abrahamu. Adamuitana, adati, “Abrahamu!” Ndipo Abrahamu adayankha kuti, “Ee Ambuye.”
Gen. 22:1 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
7
Gen. 22:11
Koma mngelo wa Chauta adamuitana kuchokera kumwamba, adati, “Abrahamu, Abrahamu!” Iye adayankha kuti, “Ee, Ambuye!” Mngeloyo adati
Gen. 22:11 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
8
Gen. 22:15-16
Mngelo wa Chauta uja adamuitana Abrahamu kachiŵiri kuchokera kumwamba, adati, “Chauta akunena kuti, ‘Ndikulumbira kuti ndidzakudalitsa kwambiri iwe chifukwa wachita zimenezi, osandimana mwana wako mmodzi yekha uja.
Gen. 22:15-16 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
9
Gen. 22:9
Atafika ku malo amene adaamuuza Mulungu aja, Abrahamu adamanga guwa, naika nkhuni pamwamba pa guwalo. Kenaka adamanga mwana wake uja, namgoneka pamwamba pa nkhunizo.
Gen. 22:9 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
ಮುಖಪುಟ
ಬೈಬಲ್
ಯೋಜನೆಗಳು
ವೀಡಿಯೊಗಳು