1
Luka 6:38
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Perekani ndipo mudzapatsidwa. Adzakupatsani mʼthumba mwanu muyeso wabwino, wotsenderezeka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Pakuti muyeso umene mumagwiritsa ntchito, ndi omwewo adzakuyeserani.”
ប្រៀបធៀប
រុករក Luka 6:38
2
Luka 6:45
Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
រុករក Luka 6:45
3
Luka 6:35
Koma kondani adani anu, achitireni zabwino, akongozeni koma osayembekezera kulandira kanthu. Pamenepo mphotho yanu idzakhala yayikulu ndipo inu mudzakhala ana a Wammwambamwamba, chifukwa ndi wokoma mtima kwa anthu osayamika ndi oyipa.
រុករក Luka 6:35
4
Luka 6:36
Khalani achifundo, monga momwe Atate anu ali achifundo.”
រុករក Luka 6:36
5
Luka 6:37
“Musaweruze, ndipo inu simudzaweruzidwa. Musatsutse ndipo inu simudzatsutsidwa. Khululukirani ena ndipo mudzakhululukidwa.
រុករក Luka 6:37
6
Luka 6:27-28
“Koma Ine ndikuwuza inu amene mukundimva: Kondani adani anu, chitirani zabwino amene amakudani. Dalitsani amene amakutembererani, apempherereni amene amakusautsani.
រុករក Luka 6:27-28
7
Luka 6:31
Inu muwachitire anthu ena, zomwe mukanafuna kuti iwo akuchitireni.
រុករក Luka 6:31
8
Luka 6:29-30
Ngati wina akumenyani patsaya limodzi mupatseninso tsaya linalo. Ngati wina akulanda mwinjiro wako, umulole atenge ndi mkanjo omwe. Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.
រុករក Luka 6:29-30
9
Luka 6:43
Palibe mtengo wabwino umene umabala chipatso choyipa, kapena mtengo oyipa umene umabala chipatso chabwino.
រុករក Luka 6:43
10
Luka 6:44
Mtengo uliwonse umadziwika ndi chipatso chake. Anthu sathyola nkhuyu pa mtengo waminga, kapena mphesa pa nthungwi.
រុករក Luka 6:44
ទំព័រដើម
ព្រះគម្ពីរ
គម្រោងអាន
វីដេអូ