1
Yoh. 3:16
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Mulungutu adaŵakonda kwambiri anthu a pa dziko lonse lapansi. Anali naye Mwana mmodzi yekha, komabe adampereka kuti aliyense wokhulupirira Iyeyo asatayike, koma akhale ndi moyo wosatha.
Compare
Yoh. 3:16 ખોજ કરો
2
Yoh. 3:17
Mulungu adatuma Mwana wakeyo pansi pano, osati kuti adzazenge anthu mlandu, koma kuti adzaŵapulumutse.
Yoh. 3:17 ખોજ કરો
3
Yoh. 3:3
Yesu adati, “Ndithu ndikunenetsa kuti ngati munthu sabadwanso kwatsopano, sangauwone Ufumu wa Mulungu.”
Yoh. 3:3 ખોજ કરો
4
Yoh. 3:18
“Munthu wokhulupirira Mwanayo, sazengedwa mlandu. Koma wosakhulupirira, wazengedwa kale, chifukwa sadakhulupirire Mwana mmodzi yekha uja wa Mulungu.
Yoh. 3:18 ખોજ કરો
5
Yoh. 3:19
Mlandu wake ndi uwu wakuti ngakhale kuŵala kudadza pansi pano, anthu adakonda mdima, osati kuŵalako, chifukwa zochita zao zinali zoipa.
Yoh. 3:19 ખોજ કરો
6
Yoh. 3:30
Iye uja ayenera kumakula, ine nkumachepa.”
Yoh. 3:30 ખોજ કરો
7
Yoh. 3:20
Aliyense wochita zoipa, amadana ndi kuŵala. Saonekera poyera, kuwopa kuti zochita zakezo zingaonekere.
Yoh. 3:20 ખોજ કરો
8
Yoh. 3:36
Munthu wokhulupirira Mwanayo, ali ndi moyo wosatha. Koma wokana kukhulupirira Mwanayo, sadzaona moyo, chifukwa chilango cha Mulungu chili pa iye.”
Yoh. 3:36 ખોજ કરો
9
Yoh. 3:14
“Monga momwe Mose adaapachikira njoka pa mtengo m'chipululu muja, momwemonso Mwana wa Munthu ayenera kudzapachikidwa
Yoh. 3:14 ખોજ કરો
10
Yoh. 3:35
Mulungu Atate amakonda Mwana wake, ndipo adaika zonse m'manja mwake.
Yoh. 3:35 ખોજ કરો
હોમ
બાઇબલ
યોજનાઓ
વિડિઓઝ