1
Yohane 15:5
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
“Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu.
Karşılaştır
Yohane 15:5 keşfedin
2
Yohane 15:4
Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.
Yohane 15:4 keşfedin
3
Yohane 15:7
Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa.
Yohane 15:7 keşfedin
4
Yohane 15:16
Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
Yohane 15:16 keşfedin
5
Yohane 15:13
Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
Yohane 15:13 keşfedin
6
Yohane 15:2
Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri.
Yohane 15:2 keşfedin
7
Yohane 15:12
Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’
Yohane 15:12 keşfedin
8
Yohane 15:8
Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.
Yohane 15:8 keşfedin
9
Yohane 15:1
“Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda.
Yohane 15:1 keşfedin
10
Yohane 15:6
Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa.
Yohane 15:6 keşfedin
11
Yohane 15:11
Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira.
Yohane 15:11 keşfedin
12
Yohane 15:10
Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo.
Yohane 15:10 keşfedin
13
Yohane 15:17
Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’
Yohane 15:17 keşfedin
14
Yohane 15:19
Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani.
Yohane 15:19 keşfedin
Ana Sayfa
Kutsal Kitap
Okuma Planları
Videolar