1
Yoh. 10:10
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Wakuba amangodzera kuba, kupha ndi kuwononga. Koma Ine ndidabwera kuti nkhosazo zikhale ndi moyo, moyo wake wochuluka.
Paghambingin
I-explore Yoh. 10:10
2
Yoh. 10:11
“Ine ndine mbusa wabwino. Mbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake.
I-explore Yoh. 10:11
3
Yoh. 10:27
Nkhosa zanga zimamva mau anga. Ine ndimazidziŵa, ndipo zimanditsatira.
I-explore Yoh. 10:27
4
Yoh. 10:28
Ndimazipatsa moyo wosatha, ndipo sizidzatayika konse. Palibe munthu wodzazilanda m'manja mwanga.
I-explore Yoh. 10:28
5
Yoh. 10:9
Khomo ndine. Munthu akaloŵera pa Ine, adzapulumuka. Azidzaloŵa ndi kutuluka, ndipo adzapeza chakudya.
I-explore Yoh. 10:9
6
Yoh. 10:14
Mbusa wabwino ndine. Nkhosa zanga ndimazidziŵa, ndipo izozo Ineyo zimandidziŵa
I-explore Yoh. 10:14
7
Yoh. 10:29-30
Atate anga amene adandipatsa nkhosazo amapambana onse, ndipo palibe amene angathe kuzilanda m'manja mwao. Ine ndi Atate ndife amodzi.”
I-explore Yoh. 10:29-30
8
Yoh. 10:15
monga momwe Atate amadziŵira Ine, nanenso nkuŵadziŵa Atatewo. Ndimatayirapo moyo wanga pa nkhosazo.
I-explore Yoh. 10:15
9
Yoh. 10:18
Palibe munthu wondilanda moyo wangawu, koma ndikuupereka ndekha. Ndili nazo mphamvu zoutaya moyo wanga, ndili nazonso mphamvu zoutenganso. Udindo umenewu ndidaulandira kwa Atate anga.”
I-explore Yoh. 10:18
10
Yoh. 10:7
Tsono Yesu adatinso, “Ndithu ndikunenetsa kuti Ine ndine khomo la nkhosa.
I-explore Yoh. 10:7
11
Yoh. 10:12
Koma wolembedwa ntchito chabe akaona mmbulu ulikudza, amazisiya nkhosazo iye nkuthaŵa. Amatero popeza kuti si mbusa weniweni, ndipo nkhosa si zake ai. Tsono mmbulu uja umagwirapo zina, zina nkumwazikana.
I-explore Yoh. 10:12
12
Yoh. 10:1
“Kunena zoona, munthu woloŵa m'khola la nkhosa osadzera pa khomo, koma kuchita kukwerera pena, ameneyo ndi wakuba ndi wolanda.
I-explore Yoh. 10:1
Home
Biblia
Mga Gabay
Mga Palabas