1
Ntc. 4:12
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Ndipo palibe wina aliyense amene angathe kupulumutsa anthu, pakuti pa dziko lonse lapansi palibe dzina lina limene Mulungu adapatsa anthu kuti tipulumuke nalo.”
Paghambingin
I-explore Ntc. 4:12
2
Ntc. 4:31
Atatha kupemphera, nyumba imene adasonkhanamo ija idayamba kugwedezeka. Onse adadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kulankhula mau a Mulungu molimba mtima.
I-explore Ntc. 4:31
3
Ntc. 4:29
Ndiye tsono Ambuye, onani zimene akutiwopsezazi, ndipo mutithandize atumiki anufe, kuti tilankhule mau anu molimba mtima ndithu.
I-explore Ntc. 4:29
4
Ntc. 4:11
Za Yesuyo mau a Mulungu akuti, “ ‘Mwala umene inu amisiri omanga nyumba mudaukana, womwewo wasanduka mwala wapangodya, wofunika koposa.’
I-explore Ntc. 4:11
5
Ntc. 4:13
Abwalo aja adazizwa poona kulimba mtima kwa Petro ndi Yohane, ndiponso podziŵa kuti anali anthu wamba, osaphunzira kwambiri. Apo adazindikira kuti anali anzake a Yesu.
I-explore Ntc. 4:13
6
Ntc. 4:32
Gulu lonse la okhulupirira linali la mtima umodzi, ndi la maganizo amodzi. Panalibe munthu amene ankati, “Zimene ndiri nazo nzangazanga,” koma aliyense ankapereka zake zonse kuti zikhale za onse.
I-explore Ntc. 4:32
Home
Biblia
Mga Gabay
Mga Palabas