1
Gen. 19:26
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Koma mkazi wa Loti adaacheukira m'mbuyo, ndiye pomwepo adasanduka mwala wamchere.
เปรียบเทียบ
สำรวจ Gen. 19:26
2
Gen. 19:16
Koma Loti ankakayikabe, tsono Chauta adamumvera chifundo. Motero anthuwo adatenga Loti, mkazi wake ndi ana ake aŵiri aja moŵagwira pa dzanja, naŵatulutsa mumzindamo, nkuŵasiya panja pomwepo.
สำรวจ Gen. 19:16
3
Gen. 19:17
Ataŵatulutsira kunja kwa mzindawo, mmodzi mwa angelowo adati, “Thamangani, mupulumutse moyo wanu. Musacheukire m'mbuyo, ndipo musaime m'chigwamo. Thaŵirani ku mapiri kuti mungaphedwe.”
สำรวจ Gen. 19:17
4
Gen. 19:29
Motero pamene Chauta ankaononga mizinda yam'chigwayo, adakumbukira pemphero la Abrahamu, ndipo adapulumutsa Loti ku chiwonongeko chimene chidasakaza mizinda ija m'mene Loti ankakhala.
สำรวจ Gen. 19:29
หน้าหลัก
พระคัมภีร์
แผนการอ่านต่างๆ
วิดีโอ