1
Luka 6:38
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Perekani ndipo mudzapatsidwa. Adzakupatsani mʼthumba mwanu muyeso wabwino, wotsenderezeka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Pakuti muyeso umene mumagwiritsa ntchito, ndi omwewo adzakuyeserani.”
සසඳන්න
Luka 6:38 ගවේෂණය කරන්න
2
Luka 6:45
Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
Luka 6:45 ගවේෂණය කරන්න
3
Luka 6:35
Koma kondani adani anu, achitireni zabwino, akongozeni koma osayembekezera kulandira kanthu. Pamenepo mphotho yanu idzakhala yayikulu ndipo inu mudzakhala ana a Wammwambamwamba, chifukwa ndi wokoma mtima kwa anthu osayamika ndi oyipa.
Luka 6:35 ගවේෂණය කරන්න
4
Luka 6:36
Khalani achifundo, monga momwe Atate anu ali achifundo.”
Luka 6:36 ගවේෂණය කරන්න
5
Luka 6:37
“Musaweruze, ndipo inu simudzaweruzidwa. Musatsutse ndipo inu simudzatsutsidwa. Khululukirani ena ndipo mudzakhululukidwa.
Luka 6:37 ගවේෂණය කරන්න
6
Luka 6:27-28
“Koma Ine ndikuwuza inu amene mukundimva: Kondani adani anu, chitirani zabwino amene amakudani. Dalitsani amene amakutembererani, apempherereni amene amakusautsani.
Luka 6:27-28 ගවේෂණය කරන්න
7
Luka 6:31
Inu muwachitire anthu ena, zomwe mukanafuna kuti iwo akuchitireni.
Luka 6:31 ගවේෂණය කරන්න
8
Luka 6:29-30
Ngati wina akumenyani patsaya limodzi mupatseninso tsaya linalo. Ngati wina akulanda mwinjiro wako, umulole atenge ndi mkanjo omwe. Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.
Luka 6:29-30 ගවේෂණය කරන්න
9
Luka 6:43
Palibe mtengo wabwino umene umabala chipatso choyipa, kapena mtengo oyipa umene umabala chipatso chabwino.
Luka 6:43 ගවේෂණය කරන්න
10
Luka 6:44
Mtengo uliwonse umadziwika ndi chipatso chake. Anthu sathyola nkhuyu pa mtengo waminga, kapena mphesa pa nthungwi.
Luka 6:44 ගවේෂණය කරන්න
නිවස
බයිබලය
සැලසුම්
වීඩියෝ