1
Luka 12:40
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”
සසඳන්න
Luka 12:40 ගවේෂණය කරන්න
2
Luka 12:31
Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.
Luka 12:31 ගවේෂණය කරන්න
3
Luka 12:15
Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”
Luka 12:15 ගවේෂණය කරන්න
4
Luka 12:34
Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”
Luka 12:34 ගවේෂණය කරන්න
5
Luka 12:25
Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula?
Luka 12:25 ගවේෂණය කරන්න
6
Luka 12:22
Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala.
Luka 12:22 ගවේෂණය කරන්න
7
Luka 12:7
Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.
Luka 12:7 ගවේෂණය කරන්න
8
Luka 12:32
“Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu.
Luka 12:32 ගවේෂණය කරන්න
9
Luka 12:24
Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame.
Luka 12:24 ගවේෂණය කරන්න
10
Luka 12:29
Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa.
Luka 12:29 ගවේෂණය කරන්න
11
Luka 12:28
Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa!
Luka 12:28 ගවේෂණය කරන්න
12
Luka 12:2
Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika.
Luka 12:2 ගවේෂණය කරන්න
නිවස
බයිබලය
සැලසුම්
වීඩියෝ