1
YOHANE 6:35
Buku Lopatulika
Yesu anati kwa iwo, Ine ndine mkate wamoyo; iye amene adza kwa Ine sadzamva njala, ndi iye amene akhulupirira Ine sadzamva ludzu nthawi zonse.
සසඳන්න
YOHANE 6:35 ගවේෂණය කරන්න
2
YOHANE 6:63
Wopatsa moyo ndi mzimu; thupi silithandiza konse. Mau amene ndalankhula ndi inu ndiwo mzimu, ndi moyo.
YOHANE 6:63 ගවේෂණය කරන්න
3
YOHANE 6:27
Gwirani ntchito si chifukwa cha chakudya chimene chitayika koma cha chakudya chimene chitsalira kumoyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani inu; pakuti ameneyo Atate, ndiye Mulungu, adamlembera chizindikiro.
YOHANE 6:27 ගවේෂණය කරන්න
4
YOHANE 6:40
Pakuti chifuniro cha Atate wanga ndi ichi, kuti yense wakuyang'ana Mwana, ndi kukhulupirira Iye, akhale nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.
YOHANE 6:40 ගවේෂණය කරන්න
5
YOHANE 6:29
Yesu anayankha nati kwa iwo, Ntchito ya Mulungu ndi iyi, kuti mukhulupirire Iye amene Iyeyo anamtuma.
YOHANE 6:29 ගවේෂණය කරන්න
6
YOHANE 6:37
Chinthu chonse chimene anandipatsa Ine Atate chidzadza kwa Ine; ndipo wakudza kwa Ine sindidzamtaya iye kunja.
YOHANE 6:37 ගවේෂණය කරන්න
7
YOHANE 6:68
Simoni Petro anamyankha Iye, Ambuye, tidzamuka kwa yani? Inu muli nao mau a moyo wosatha.
YOHANE 6:68 ගවේෂණය කරන්න
8
YOHANE 6:51
Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.
YOHANE 6:51 ගවේෂණය කරන්න
9
YOHANE 6:44
Kulibe mmodzi akhoza kudza kwa Ine koma ngati Atate wondituma Ine amkoka iye; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.
YOHANE 6:44 ගවේෂණය කරන්න
10
YOHANE 6:33
Pakuti mkate wa Mulungu ndiye wakutsika kuchokera Kumwamba ndi kupatsa moyo kwa dziko lapansi.
YOHANE 6:33 ගවේෂණය කරන්න
11
YOHANE 6:48
Ine ndine mkate wamoyo.
YOHANE 6:48 ගවේෂණය කරන්න
12
YOHANE 6:11-12
Pomwepo Yesu anatenga mikateyo; ndipo pamene adayamika, anagawira iwo akukhala pansi; momwemonso ndi tinsomba, monga momwe iwo anafuna. Ndipo pamene adakhuta, Iye ananena kwa ophunzira ake, Sonkhanitsani makombo kuti kasatayike kanthu.
YOHANE 6:11-12 ගවේෂණය කරන්න
13
YOHANE 6:19-20
Ndipo pamene adapalasa monga mastadiya makumi awiri ndi asanu kapena makumi atatu, anaona Yesu alikuyenda panyanja, ndi kuyandikira ngalawa; ndipo anachita mantha. Koma Iye ananena nao, Ndine; musaope.
YOHANE 6:19-20 ගවේෂණය කරන්න
නිවස
බයිබලය
සැලසුම්
වීඩියෝ