1
Lk. 23:34
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Yesu adati, “Atate, muŵakhululukire anthuŵa, chifukwa sakudziŵa zimene akuchita.” Iwo aja adagaŵana zovala zake pakuchita maere.
နှိုင်းယှဉ်
Lk. 23:34ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
2
Lk. 23:43
Yesu adamuyankha kuti, “Ndithu ndikunenetsa kuti lero lomwe lino ukhala nane ku Malo a Chisangalalo, Kumwamba.”
Lk. 23:43ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
3
Lk. 23:42
Ndipo adati, “Inu, mukandikumbikire mukakafika mu Ufumu wanu.”
Lk. 23:42ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
4
Lk. 23:46
Tsono Yesu adanena mokweza mau kuti, “Atate ndikupereka mzimu wanga m'manja mwanu.” Atanena zimenezi, adatsirizika.
Lk. 23:46ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
5
Lk. 23:33
Pamene adafika ku malo otchedwa Chibade cha Mutu, adapachika Yesu komweko pa mtanda. Komwekonso adapachika zigaŵenga zija, china ku dzanja lamanja, china ku dzanja lamanzere.
Lk. 23:33ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
6
Lk. 23:44-45
Nthaŵi itakwana ngati 12 koloko masana, padaagwa mdima pa dziko lonse mpaka pa 3 koloko, dzuŵa litangoti bii kuda. Pamenepo chinsalu chochinga chija cha m'Nyumba ya Mulungu chidang'ambika pakatimpakati.
Lk. 23:44-45ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
7
Lk. 23:47
Mkulu wa asilikali ataona zimene zidaachitikazo, adatamanda Mulungu, adati, “Ndithudi munthuyu adaalidi wosalakwa konse.”
Lk. 23:47ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
ပင်မစာမျက်နှာ
ကျမ်းစာ
အစီအစဉ်
ဗီဒီယို