1
Yoh. 10:10
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Wakuba amangodzera kuba, kupha ndi kuwononga. Koma Ine ndidabwera kuti nkhosazo zikhale ndi moyo, moyo wake wochuluka.
နှိုင်းယှဉ်
Yoh. 10:10ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
2
Yoh. 10:11
“Ine ndine mbusa wabwino. Mbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake.
Yoh. 10:11ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
3
Yoh. 10:27
Nkhosa zanga zimamva mau anga. Ine ndimazidziŵa, ndipo zimanditsatira.
Yoh. 10:27ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
4
Yoh. 10:28
Ndimazipatsa moyo wosatha, ndipo sizidzatayika konse. Palibe munthu wodzazilanda m'manja mwanga.
Yoh. 10:28ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
5
Yoh. 10:9
Khomo ndine. Munthu akaloŵera pa Ine, adzapulumuka. Azidzaloŵa ndi kutuluka, ndipo adzapeza chakudya.
Yoh. 10:9ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
6
Yoh. 10:14
Mbusa wabwino ndine. Nkhosa zanga ndimazidziŵa, ndipo izozo Ineyo zimandidziŵa
Yoh. 10:14ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
7
Yoh. 10:29-30
Atate anga amene adandipatsa nkhosazo amapambana onse, ndipo palibe amene angathe kuzilanda m'manja mwao. Ine ndi Atate ndife amodzi.”
Yoh. 10:29-30ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
8
Yoh. 10:15
monga momwe Atate amadziŵira Ine, nanenso nkuŵadziŵa Atatewo. Ndimatayirapo moyo wanga pa nkhosazo.
Yoh. 10:15ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
9
Yoh. 10:18
Palibe munthu wondilanda moyo wangawu, koma ndikuupereka ndekha. Ndili nazo mphamvu zoutaya moyo wanga, ndili nazonso mphamvu zoutenganso. Udindo umenewu ndidaulandira kwa Atate anga.”
Yoh. 10:18ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
10
Yoh. 10:7
Tsono Yesu adatinso, “Ndithu ndikunenetsa kuti Ine ndine khomo la nkhosa.
Yoh. 10:7ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
11
Yoh. 10:12
Koma wolembedwa ntchito chabe akaona mmbulu ulikudza, amazisiya nkhosazo iye nkuthaŵa. Amatero popeza kuti si mbusa weniweni, ndipo nkhosa si zake ai. Tsono mmbulu uja umagwirapo zina, zina nkumwazikana.
Yoh. 10:12ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
12
Yoh. 10:1
“Kunena zoona, munthu woloŵa m'khola la nkhosa osadzera pa khomo, koma kuchita kukwerera pena, ameneyo ndi wakuba ndi wolanda.
Yoh. 10:1ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
ပင်မစာမျက်နှာ
ကျမ်းစာ
အစီအစဉ်
ဗီဒီယို