1
Gen. 15:6
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
Apo Abramu adakhulupirira Chauta, ndipo chifukwa cha chimenecho, Chauta adamuwona kuti ndi wolungama.
နှိုင်းယှဉ်
Gen. 15:6ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
2
Gen. 15:1
Zitatha izi, Chauta adaonekera Abramu m'masomphenya namuuza kuti, “Usachite mantha Abramu, Ine ndili ngati chishango chako chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yaikulu.”
Gen. 15:1ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
3
Gen. 15:5
Pomwepo Chauta adatulutsira Abramu panja, namuuza kuti, “Tayang'ana kuthamboku, ndipo uŵerenge nyenyezizo ngati ungathe. Iwe udzakhala ndi zidzukulu zochuluka ngati nyenyezizo.”
Gen. 15:5ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
4
Gen. 15:4
Tsono Chauta adamuuza kuti, “Uyu sadzalandira chuma chako kukhala choloŵa chake. Yemwe adzalandire chuma chakochi ndi mwana wako weniweni.”
Gen. 15:4ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
5
Gen. 15:13
Chauta adamuuza kuti, “Udziŵe ndithu kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo m'dziko la eni. Zidzakhala akapolo kumeneko, ndipo zidzazunzika zaka zokwanira 400.
Gen. 15:13ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
6
Gen. 15:2
Koma Abramu adati, “Ambuye Chauta, ine ndilibe ana. Tsono mungathe bwanji kundipatsa mphotho? Woloŵa m'malo mwanga ndi Eliyezere wa ku Damasikoyu.
Gen. 15:2ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
7
Gen. 15:18
Pa tsiku limeneli mpamene Chauta adachita chipangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapatsa zidzukulu zako dziko lonseli kuyambira ku mtsinje wa ku Ejipito mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
Gen. 15:18ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
8
Gen. 15:16
Patapita mibadwo inai, zidzukulu zakozo zidzabwereranso, chifukwa sindidzaŵathamangitsa Aamori mpaka kuipa kwao kutafika pachimake penipeni kuti adzalangidwe.”
Gen. 15:16ရှာဖွေလေ့လာလိုက်ပါ။
ပင်မစာမျက်နှာ
သမ္မာကျမ်းစာ
အစီအစဉ်များ
ဗီဒီယိုများ