LUKA 3:4-6
LUKA 3:4-6 BLP-2018
monga mwalembedwa m'buku la Yesaya mneneri, kuti, Mau a wofuula m'chipululu, konzani khwalala la Ambuye, lungamitsani njira zake. Chigwa chilichonse chidzadzazidwa, ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzachepsedwa; ndipo zokhota zidzakhala zolungama, ndipo njira za zigoloondo zidzakhala zosalala; ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.