1
YOHANE 6:35
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
Yesu anati kwa iwo, Ine ndine mkate wamoyo; iye amene adza kwa Ine sadzamva njala, ndi iye amene akhulupirira Ine sadzamva ludzu nthawi zonse.
Palyginti
Naršyti YOHANE 6:35
2
YOHANE 6:63
Wopatsa moyo ndi mzimu; thupi silithandiza konse. Mau amene ndalankhula ndi inu ndiwo mzimu, ndi moyo.
Naršyti YOHANE 6:63
3
YOHANE 6:27
Gwirani ntchito si chifukwa cha chakudya chimene chitsalira kumoyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani inu; pakuti ameneyo Atate, ndiye Mulungu, adamlembera chizindikiro.
Naršyti YOHANE 6:27
4
YOHANE 6:40
Pakuti chifuniro cha Atate wanga ndi ichi, kuti yense wakuyang'ana Mwana, ndi kukhulupirira Iye, akhale nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.
Naršyti YOHANE 6:40
5
YOHANE 6:29
Yesu anayankha nati kwa iwo, Ntchito ya Mulungu ndi iyi, kuti mukhulupirire Iye amene Iyeyo anamtuma.
Naršyti YOHANE 6:29
6
YOHANE 6:37
Chinthu chonse chimene anandipatsa Ine Atate chidzadza kwa Ine; ndipo wakudza kwa Ine sindidzamtaya iye kunja.
Naršyti YOHANE 6:37
7
YOHANE 6:68
Simoni Petro anamyankha Iye, Ambuye, tidzamuka kwa yani? Inu muli nao mau a moyo wosatha.
Naršyti YOHANE 6:68
8
YOHANE 6:51
Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.
Naršyti YOHANE 6:51
9
YOHANE 6:44
Kulibe mmodzi akhoza kudza kwa Ine koma ngati Atate wondituma Ine amkoka iye; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.
Naršyti YOHANE 6:44
10
YOHANE 6:33
Pakuti mkate wa Mulungu ndiye wakutsika kuchokera Kumwamba ndi kupatsa moyo kwa dziko lapansi.
Naršyti YOHANE 6:33
11
YOHANE 6:48
Ine ndine mkate wamoyo.
Naršyti YOHANE 6:48
12
YOHANE 6:11-12
Pomwepo Yesu anatenga mikateyo; ndipo pamene adayamika, anagawira iwo akukhala pansi; momwemonso ndi tinsomba, monga momwe iwo anafuna. Ndipo pamene adakhuta, Iye ananena kwa ophunzira ake, Sonkhanitsani makombo kuti kasatayike kanthu.
Naršyti YOHANE 6:11-12
13
YOHANE 6:19-20
Ndipo pamene adapalasa monga mastadiya makumi awiri ndi asanu kapena makumi atatu, anaona Yesu alikuyenda panyanja, ndi kuyandikira ngalawa; ndipo anachita mantha. Koma Iye ananena nao, Ndine; musaope.
Naršyti YOHANE 6:19-20
Pradžia
Biblija
Planai
Vaizdo įrašai