1
YOHANE 15:5
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zake: wakukhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye, ameneyo abala chipatso chambiri; pakuti kopanda Ine simungathe kuchita kanthu.
ತಾಳೆಮಾಡಿ
YOHANE 15:5 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
2
YOHANE 15:4
Khalani mwa Ine, ndi Ine mwa inu. Monga nthambi siingathe kubala chipatso pa yokha, ngati siikhala mwampesa; motere mulibe inunso ngati simukhala mwa Ine.
YOHANE 15:4 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
3
YOHANE 15:7
Ngati mukhala mwa Ine, ndi mau anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene muchifuna ndipo chidzachitika kwa inu.
YOHANE 15:7 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
4
YOHANE 15:16
Inu simunandisankha Ine, koma Ine ndinakusankhani inu, ndipo ndinakuikani, kuti mukamuke inu ndi kubala chipatso, ndi kuti chipatso chanu chikhale; kuti chimene chilichonse mukapempha Atate m'dzina langa akakupatseni inu.
YOHANE 15:16 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
5
YOHANE 15:13
Palibe munthu ali nacho chikondi choposa ichi, chakuti munthu ataya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
YOHANE 15:13 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
6
YOHANE 15:2
Nthambi iliyonse ya mwa Ine yosabala chipatso, aichotsa; ndi iliyonse yakubala chipatso, aisadza, kuti ikabale chipatso chochuluka.
YOHANE 15:2 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
7
YOHANE 15:12
Lamulo langa ndi ili, kuti mukondane wina ndi mnzake, monga ndakonda inu.
YOHANE 15:12 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
8
YOHANE 15:8
Mwa ichi alemekezedwa Atate wanga, kuti mubale chipatso chambiri; ndipo mudzakhala ophunzira anga.
YOHANE 15:8 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
9
YOHANE 15:1
Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam'munda.
YOHANE 15:1 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
10
YOHANE 15:6
Ngati wina sakhala mwa Ine, watayika kunja monga nthambi, nafota; ndipo azisonkhanitsa nazitaya kumoto, nazitentha.
YOHANE 15:6 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
11
YOHANE 15:11
Izi ndalankhula ndi inu, kuti chimwemwe changa chikhale mwa inu, ndi kuti chimwemwe chanu chidzale.
YOHANE 15:11 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
12
YOHANE 15:10
Ngati musunga malamulo anga mudzakhala m'chikondi changa; monga Iye ndasunga malamulo a Atate wanga, ndipo ndikhala m'chikondi chake.
YOHANE 15:10 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
13
YOHANE 15:17
Zinthu izi ndilamula inu, kuti mukondane wina ndi mnzake.
YOHANE 15:17 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
14
YOHANE 15:19
Mukadakhala a dziko lapansi, dziko lapansi likadakonda zake za lokha; koma popeza simuli a dziko lapansi, koma Ine ndinakusankhani inu mwa dziko lapansi, chifukwa cha ichi likudani inu.
YOHANE 15:19 ಅನ್ವೇಷಿಸಿ
ಮುಖಪುಟ
ಬೈಬಲ್
ಯೋಜನೆಗಳು
ವೀಡಿಯೊಗಳು