“Inunso muyenera kukhala maso chifukwa simukudziwa nthawi imene mwini nyumba adzabwere, kaya madzulo, kapena pakati pa usiku, kapena tambala akulira, kapena mʼbandakucha. Ngati atabwera mwadzidzidzi, asadzakupezeni inu muli mtulo. Zimene ndikunena kwa inu, ndikunena kwa aliyense: ‘Khalani tcheru!’ ”