1
LUKA 23:34
Buku Lopatulika
Ndipo Yesu ananena, Atate, muwakhululukire iwo, pakuti sadziwa chimene achita. Ndipo anagawana zovala zake, poyesa maere.
Bera saman
Njòttu LUKA 23:34
2
LUKA 23:43
Ndipo Iye ananena naye, Indetu, ndinena ndi iwe, Lero lino udzakhala ndine mu Paradaiso.
Njòttu LUKA 23:43
3
LUKA 23:42
Ndipo ananena, Yesu, ndikumbukireni m'mene mulowa Ufumu wanu.
Njòttu LUKA 23:42
4
LUKA 23:46
Ndipo pamene Yesu anafuula ndi mau aakulu, anati, Atate, m'manja mwanu ndipereka mzimu wanga. Ndipo pakutero anapereka mzimu wake.
Njòttu LUKA 23:46
5
LUKA 23:33
Ndipo pamene anafika kumalo dzina lake Bade, anampachika Iye pamtanda pomwepo, ndi ochita zoipa omwe, mmodzi kudzanja lamanja ndi wina kulamanzere.
Njòttu LUKA 23:33
6
LUKA 23:44-45
Ndipo ora lake pamenepo linali ngati lachisanu ndi chimodzi. Ndipo panali mdima padziko lonse kufikira ora lachisanu ndi chinai, ndipo dzuwa linada. Ndipo nsalu yotchinga ya mu Kachisi inang'ambika pakati.
Njòttu LUKA 23:44-45
7
LUKA 23:47
Ndipo pamene kenturiyo anaona chinachitikacho, analemekeza Mulungu, nanena, Zoonadi munthu uyu anali wolungama.
Njòttu LUKA 23:47
Heim
Biblía
Áætlanir
Myndbönd