1
Genesis 2:24
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
Konpare
Eksplore Genesis 2:24
2
Genesis 2:18
Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
Eksplore Genesis 2:18
3
Genesis 2:7
Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
Eksplore Genesis 2:7
4
Genesis 2:23
Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
Eksplore Genesis 2:23
5
Genesis 2:3
Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
Eksplore Genesis 2:3
6
Genesis 2:25
Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.
Eksplore Genesis 2:25
Akèy
Bib
Plan yo
Videyo