1
GENESIS 9:12-13
Buku Lopatulika
Ndipo anati Mulungu, Ichi ndi chizindikiro cha pangano limene ndipangana ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse zili pamodzi ndi inu, ku mibadwomibadwo; ndiika utawaleza wanga m'mtambomo, ndipo udzakhala chizindikiro cha pangano lopangana ndi Ine ndi dziko lapansi.
Vertaa
Tutki GENESIS 9:12-13
2
GENESIS 9:16
Ndipo utawo udzakhala m'mtambo; ndipo ndidzauyang'anira kuti ndikumbukire pangano lachikhalire lili ndi Mulungu ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo padziko lapansi.
Tutki GENESIS 9:16
3
GENESIS 9:6
Amene akhetsa mwazi wa munthu, ndi munthunso mwazi wake udzakhetsedwa: chifukwa m'chifanizo cha Mulungu Iye anampanga munthu.
Tutki GENESIS 9:6
4
GENESIS 9:1
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake, nati kwa iwo, Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi.
Tutki GENESIS 9:1
5
GENESIS 9:3
Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.
Tutki GENESIS 9:3
6
GENESIS 9:2
Kuopsa kwanu, ndi kuchititsa mantha kwanu kudzakhala pa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi pa zouluka zonse za m'mlengalenga, ndi pa zonse zokwawa pansi, ndi pansomba zonse za m'nyanja, zapatsidwa m'dzanja lanu.
Tutki GENESIS 9:2
7
GENESIS 9:7
Ndi inu, mubalane, muchuluke; muswane padziko lapansi, nimuchuluke m'menemo.
Tutki GENESIS 9:7
Koti
Raamattu
Suunnitelmat
Videot