Iwo atamaliza kudya chakudya chammawa, Yesu anati kwa Simoni Petro, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikonda Ine kuposa mmene amandikondera awa?”
Iye anati, “Inde Ambuye, Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.”
Yesu anati, “Samala ana ankhosa anga.”
Yesu anatinso, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?”
Iye anayankha kuti, “Inde, Ambuye, Inu mukudziwa kuti ine ndimakukondani.”
Yesu anati, “Weta nkhosa zanga.”
Yesu anati kwa iye kachitatu, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?”
Petro anadzimvera chisoni chifukwa Yesu anamufunsa kachitatu kuti, “Kodi umandikonda Ine?” Iye anati, “Ambuye, Inu mudziwa zinthu zonse. Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.”
Yesu anati, “Dyetsa nkhosa zanga.