1
Genesis 37:5
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Tsiku lina Yosefe analota maloto ndipo pamene anawuza abale ake za malotowo, iwo anawonjeza kumuda.
Compare
Explore Genesis 37:5
2
Genesis 37:3
Tsono Israeli ankakonda Yosefe koposa ana ake ena onse, chifukwa anali mwana wobadwa muukalamba wake. Ndipo anamusokera mkanjo wa manja aatali.
Explore Genesis 37:3
3
Genesis 37:4
Pamene abale ake anaona kuti abambo awo ankakonda Yosefe kuposa aliyense wa iwo, anayamba kumuda Yosefe ndipo sankayankhula naye zamtendere.
Explore Genesis 37:4
4
Genesis 37:9
Tsiku lina analotanso maloto ena, ndipo anafotokozera abale ake za malotowo. Iye anati, “Tamverani, ndinalotanso maloto ena. Ulendo uno dzuwa ndi mwezi pamodzi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zimandigwadira.”
Explore Genesis 37:9
5
Genesis 37:11
Abale ake anamuchitira nsanje, koma abambo ake anasunga nkhaniyi mu mtima.
Explore Genesis 37:11
6
Genesis 37:6-7
Iye anawawuza kuti, “Tamvani maloto amene ndinalota: Ife timamanga mitolo ya tirigu ku munda ndipo mwadzidzidzi mtolo wanga unayimirira chilili, pamene mitolo yanu inazungulira mtolo wangawo nʼkumawugwadira.”
Explore Genesis 37:6-7
7
Genesis 37:20
Tsono tiyeni timuphe ndi kuponya thupi lake mu chimodzi mwa zitsime izi ndipo tidzati anadyedwa ndi nyama zakuthengo zolusa. Tsono timuonera zomwe ziti zichitike ndi maloto ake aja.”
Explore Genesis 37:20
8
Genesis 37:28
Amalonda ena a ku Midiyani ankadutsa pomwepo. Tsono abale ake a Yosefe anamutulutsa Yosefe uja mu chitsime chija ndipo anamugulitsa kwa Aismaeli aja pamtengo wa masekeli makumi awiri. Choncho anapita naye Yosefe ku Igupto.
Explore Genesis 37:28
9
Genesis 37:19
Iwo anawuzana nati, “Uyo akubwera apo wamaloto uja.
Explore Genesis 37:19
10
Genesis 37:18
Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.
Explore Genesis 37:18
11
Genesis 37:22
tisakhetse magazi. Tiyeni timuponye mʼchitsime ku chipululu konkuno. Koma tisamuvulaze nʼkomwe. Rubeni ananena zonsezi kuti apulumutse Yosefe ndi kuti pambuyo pake akamupereke kwa abambo awo.”
Explore Genesis 37:22
Home
Bible
Plans
Videos