Kenaka anadalitsa Yosefe nati,
“Mulungu amene makolo anga
Abrahamu ndi Isake anamutumikira,
Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga
moyo wanga wonse kufikira lero,
mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse,
ameneyo adalitse anyamata awa.
Kudzera mwa iwowa
dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka.
Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu
pa dziko lapansi.”